Tuesday, November 16, 2010

Ayamikira boma pochepetsa umbanda wamfuti

WOLEMBA RICHARD CHIROMBO


Bungwe laPeople’s Federation for National Peace and Development

(Pefenap), lomwe limalimbikitsa zabata ndimtendere, layamikira unduna

woyang’anira zachitetezo chaanthu polimbikitsa ntchito zothana

ndiumbanda wamfuti, chinthu chomwe akuti chingapangitse kuti madera

akumidzi atukuke mwachangu.

Mkulu wabungweli, aEdward Chaka, adati kafukufuku yemwe bungwe lawo

lidachita miyezi isanu yapitayi waonetsa kuti m’chitidwe okuba

moopseza ndimfuti wachepa nditheka, chinthu chomwe adati chilimbikitsa

anthu omwe alindintchito zamalonda m’matauni kuganiza zopita kumidzi

popeza chitetezo Chayamba kukhwima m’madera onse.

“M’chitidwe okuba ndimfuti umabwezeretsa chitukuko m’mbuyo. Ngakhale

anthu ena amalonda akudandaula kuti umbanda wamfuti ukuopseza

chitetezo, makamaka chaAmalawi achimwenye, kafukufuku wathu waonetsa

kuti zinthu ziliko bwino kusiyana ndimomwe zidalili zaka zinayi

zapitazo,” adatero aChaka.

Mkuluyu adawonjezera kuti anthu ngakhale amwenye ambiri omwe

adafunsidwa zamaganizo awo adasonjeza kukhutira ndichitetezo, ngakhale

ambiri ayiwo adapempha kuti ogwira ntchito zachitetezo

asamangokhwimitsa chitetezo masana okha, popeza ntchito zambiri

zaumbanda zimachitikanso usiku.

No comments: