Tuesday, November 16, 2010

Apempha boma lilimbikitse ntchito zaumoyo

WOLEMBA RICHARD CHIROMBO


Mgwirizano wamabungwe olimbikitsa ntchito zaumoyo m’dziko muno,

laMalawi Heath Equity Network (MHEN), lapempha boma kuti libwezeretse

zinthu zina zomwe zimalimbikitsa ntchito zaumoyo ngati likufuna kuti

mzika zake zipitilire kukhala zathanzi.

Oyang’anira ntchito zaMHEN m’dziko muno, aMartha Kwataine, adati,

mwazina, kuchotsa kwandalama zomwe unduna wazaumoyo umapereka kwaana

omwe amaphunzira zaunamwino ndiudotolo m’sukulu zam’dziko muno

kungapangitse kuti ntchito zaumoyo zibwerere pansi.

“M’mene zilili panopa, ana ambiri sazikwanitsa kupeza ndalama

zolipilira maphunziro aunamwino ndiudotolo, chinthu chomwe chipangitse

kuti anthu ogwira ntchito zamtunduwu achepe,” adatero aKwataine.

Iwo adati zimenezi zionjezeranso pamavuto omwe alipo kale m’dziko

muno, ndipo adatchulapo zazinthu monga kusowa kwandalama zokonzera

zipatala, kuchepa kwaanthu ogwira ntchitozi, komanso kutaya anthu

aluso lawo omwe akumakhamukira kuzipatala zakunja kukagwira ntchito

zamalipiro apamwamba.

Panthawi yomwe unduna wazaumoyo udalengeza kuti wasiya kuonjezera

kangachepe kundalama zomwe anthu opanga zaunamwino ndiudotolo ama

No comments: